18 Ndiyeno Yeremiya anauza anthu a m’nyumba ya Rekabu kuti: “Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Chifukwa chakuti mwamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu,+ ndipo mukupitiriza kusunga malamulo ake onse ndi kuchita zonse zimene anakulamulani,+