7 Chotero, akuluakulu a ku Mowabu ndi a ku Midiyani anapita kwa Balamu+ atatenga malipiro okamulipira kuti awawombezere maula,+ komanso anamuuza zimene Balaki ananena.
12 Pakuti aliyense wochita zimenezi ndi wonyansa kwa Yehova. Ndipo chifukwa chakuti anthu a mitundu ina akuchita zimenezi, Yehova Mulungu wako akuwapitikitsa pamaso pako.+