2 “Ana a Isiraeli azikhoma mahema awo, aliyense azikhoma hema wake m’chigawo chawo cha mafuko atatu,+ potsata chizindikiro cha nyumba ya makolo ake. Azikhoma mahema awo mozungulira chihema chokumanako komanso moyang’ana chihemacho.
34 Ana a Isiraeli anachita zonse monga mmene Yehova analamulira Mose.+ Dongosolo limene analitsatira pomanga misasa yawo m’zigawo za mafuko atatu,+ n’limenenso anatsatira posamuka,+ aliyense m’banja lake malinga ndi nyumba ya makolo ake.