15 “Muzipha chiweto chanu ndi kudya nyama yake nthawi iliyonse imene mwafuna.+ Muzidya nyamayo malinga ndi dalitso limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani m’mizinda yanu yonse. Munthu wodetsedwa+ komanso munthu woyera ali ndi ufulu wakudya nyamayo, monga mmene amadyera insa ndi mbawala yamphongo.+