2 Tsopano Yoswa anatumiza amuna ena kuchokera ku Yeriko kupita ku Ai,+ pafupi ndi Beti-aveni,+ kum’mawa kwa Beteli.+ Iye anawauza kuti: “Pitani kumeneko, mukazonde dzikolo.” Amunawo anapita, n’kukazonda dziko la Ai.+
12 Malire a gawo lawo kumpoto anayambira ku Yorodano, n’kupitirira kukafika kumalo otsetsereka a kumpoto kwa Yeriko,+ n’kukwera phiri chakumadzulo, n’kukathera kuchipululu cha Beti-aveni.+