6 M’mbali mwa nyumbayo munali mizere itatu ya zipinda zosanjikizana. Mzere uliwonse unali ndi zipinda 30. Zipinda zam’mbali kuzungulira nyumbayo zinali kulowa ku khoma la nyumbayo kuti zikhale ndi chozichirikiza. Koma sizinachirikizike ndi khoma la nyumbayo.+