2 Chotero iye anapita kukaonekera kwa Asa n’kumuuza kuti: “Tamverani mfumu Asa ndi anthu onse a fuko la Yuda ndi Benjamini. Yehova akhala nanu inuyo mukapitiriza kukhala naye.+ Mukamufunafuna+ iye adzalola kuti mum’peze, koma mukamusiya nayenso adzakusiyani.+
6 Ndiponso, popanda chikhulupiriro+ n’zosatheka kukondweretsa Mulungu.+ Pakuti aliyense wofika kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti iye alikodi,+ ndi kuti amapereka mphoto+ kwa anthu omufunafuna ndi mtima wonse.+