Deuteronomo 2:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Lero ndichititsa anthu a mitundu ina okhala pansi pa thambo, amene adzamva za inu, kuchita nanu mantha kwambiri ndi kuyamba kukuopani. Chifukwa cha inu, iwo adzanthunthumira ndi kumva zopweteka zofanana ndi zowawa za pobereka.’+ Deuteronomo 11:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Palibe munthu amene adzaima kuti alimbane nanu.+ Yehova Mulungu wanu adzachititsa dziko lonse limene mudzapondapo kugwidwa ndi mantha aakulu ndi kukuopani,+ monga mmene anakulonjezerani. Yoswa 2:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Ndipo iye anauza amunawo kuti: “Ndikudziwa kuti Yehova akupatsani ndithu dziko lino.+ Ife tagwidwa ndi mantha chifukwa cha inu,+ ndipo anthu a dziko lino ataya mtima chifukwa chokuopani.+
25 Lero ndichititsa anthu a mitundu ina okhala pansi pa thambo, amene adzamva za inu, kuchita nanu mantha kwambiri ndi kuyamba kukuopani. Chifukwa cha inu, iwo adzanthunthumira ndi kumva zopweteka zofanana ndi zowawa za pobereka.’+
25 Palibe munthu amene adzaima kuti alimbane nanu.+ Yehova Mulungu wanu adzachititsa dziko lonse limene mudzapondapo kugwidwa ndi mantha aakulu ndi kukuopani,+ monga mmene anakulonjezerani.
9 Ndipo iye anauza amunawo kuti: “Ndikudziwa kuti Yehova akupatsani ndithu dziko lino.+ Ife tagwidwa ndi mantha chifukwa cha inu,+ ndipo anthu a dziko lino ataya mtima chifukwa chokuopani.+