2 Iye analima mundawo n’kuchotsamo miyala, kenako anabzalamo mphesa zofiira zabwino kwambiri. Anamanga nsanja pakati pa mundawo.+ Anasemamonso choponderamo mphesa.+ Iye anali kuyembekezera kuti mundawo ubereka mphesa zabwino,+ koma unabereka mphesa zam’tchire.+