Ekisodo 34:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 “Zipatso zoyamba kucha zabwino koposa+ za m’munda mwanu muzibwera nazo kunyumba ya Yehova Mulungu wanu.+ “Musawiritse mwana wa mbuzi mumkaka wa mayi wake.”+ Numeri 15:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 muzikapereka chopereka kwa Yehova pachakudya chilichonse cha m’dzikolo,+ chimene muzikadya. Deuteronomo 26:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 ukatenge zina mwa zipatso zoyambirira+ pa zipatso zonse za m’munda mwako zimene udzakolola m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa. Ukaziike m’dengu ndi kupita nazo kumalo amene Yehova Mulungu wako adzasankhe kuika dzina lake.+
26 “Zipatso zoyamba kucha zabwino koposa+ za m’munda mwanu muzibwera nazo kunyumba ya Yehova Mulungu wanu.+ “Musawiritse mwana wa mbuzi mumkaka wa mayi wake.”+
2 ukatenge zina mwa zipatso zoyambirira+ pa zipatso zonse za m’munda mwako zimene udzakolola m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa. Ukaziike m’dengu ndi kupita nazo kumalo amene Yehova Mulungu wako adzasankhe kuika dzina lake.+