Genesis 33:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Koma Yakobo anati: “Monga mukudziwa mbuyanga, anawa ndi osakhwima, komanso ndili ndi nkhosa ndi ng’ombe zoyamwitsa.+ Tikaziyendetsa mofulumira kwambiri, ngakhale tsiku limodzi lokha, ndithu zifa zonse.+ Ekisodo 23:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 “Uzigwira ntchito masiku 6.+ Koma tsiku la 7 usamagwire ntchito, kuti ng’ombe yako ndi bulu wako zizipuma, ndipo mwana wa kapolo wako wamkazi ndi mlendo azipumula.+ Deuteronomo 22:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 “Ukaona bulu wa m’bale wako kapena ng’ombe yake itagwa pamsewu usailekerere. Uzim’thandiza m’bale wako mwa kuidzutsa.+ Deuteronomo 22:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 “Usamange ng’ombe ndi bulu kuti uzilimitse pamodzi.+ Deuteronomo 25:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 “Usamange ng’ombe pakamwa pamene ikupuntha mbewu.+ Yona 4:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Kodi ine sindikuyenera kumvera chisoni mzinda waukulu wa Nineve,+ mmene muli anthu oposa 120,000, omwe sadziwa kusiyanitsa dzanja lawo lamanja ndi lamanzere? Kodi sindiyenera kumveranso chisoni ziweto zambiri zimene zili mmenemo?”+
13 Koma Yakobo anati: “Monga mukudziwa mbuyanga, anawa ndi osakhwima, komanso ndili ndi nkhosa ndi ng’ombe zoyamwitsa.+ Tikaziyendetsa mofulumira kwambiri, ngakhale tsiku limodzi lokha, ndithu zifa zonse.+
12 “Uzigwira ntchito masiku 6.+ Koma tsiku la 7 usamagwire ntchito, kuti ng’ombe yako ndi bulu wako zizipuma, ndipo mwana wa kapolo wako wamkazi ndi mlendo azipumula.+
4 “Ukaona bulu wa m’bale wako kapena ng’ombe yake itagwa pamsewu usailekerere. Uzim’thandiza m’bale wako mwa kuidzutsa.+
11 Kodi ine sindikuyenera kumvera chisoni mzinda waukulu wa Nineve,+ mmene muli anthu oposa 120,000, omwe sadziwa kusiyanitsa dzanja lawo lamanja ndi lamanzere? Kodi sindiyenera kumveranso chisoni ziweto zambiri zimene zili mmenemo?”+