17 Yehova adzabweretsera iweyo,+ anthu ako, ndi nyumba ya bambo ako masiku amene sanakhaleponso kuyambira tsiku limene Efuraimu anapatukana ndi Yuda.+ Iye adzakubweretserani mfumu ya Asuri.+
20 “M’tsiku limenelo, pogwiritsira ntchito lezala lobwereka la kuchigawo cha ku Mtsinje,*+ pogwiritsira ntchito mfumu ya Asuri,+ Yehova adzameta tsitsi la kumutu ndi tsitsi la m’mapazi, ndipo lezalalo lidzachotseratu ngakhale ndevu.+