Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 29:39
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Uzipereka mwana wa nkhosa mmodzi m’mawa,+ ndipo mwana wa nkhosa winayo madzulo kuli kachisisira.*+

  • Levitiko 5:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 “Munthu akachita mosakhulupirika mwa kuchimwira zinthu zopatulika za Yehova+ mosadziwa, pamenepo azibweretsa kwa Yehova nkhosa yamphongo yopanda chilema kuti ikhale nsembe yake ya kupalamula.+ Nkhosayo mtengo wake uzikhala masekeli* asiliva+ ofanana ndi sekeli la kumalo oyera* kuti ikhale nsembe ya kupalamula.

  • Levitiko 9:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Pamenepo anauza Aroni kuti: “Tenga ng’ombe yaing’ono kuti ikhale nsembe yamachimo,+ ndi nkhosa yamphongo kuti ikhale nsembe yopsereza.+ Nyama zonsezi zikhale zopanda chilema, ndipo uzipereke kwa Yehova.+

  • Numeri 6:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndipo apereke kwa Yehova nsembe ya iye mwini. Nsembeyo ikhale nkhosa yaing’ono yamphongo yopanda chilema, yosapitirira chaka chimodzi, monga nsembe yopsereza.+ Aperekenso mwana wa nkhosa wamkazi wopanda chilema, wosapitirira chaka chimodzi, monga nsembe yamachimo.+ Komanso apereke nkhosa yamphongo yopanda chilema, monga nsembe yachiyanjano.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena