15 Kodi iwo anachita manyazi chifukwa chochita zinthu zonyansazi?+ Iwo sanachite manyazi ngakhale pang’ono, komanso sadziwa n’komwe kuchita manyazi.+ Choncho iwo adzagwa pamodzi ndi anthu amene akugwa.+ Pamene ndidzakhala ndikuwaimba mlandu adzapunthwa,” watero Yehova.