8 “‘Chotero mofanana ndi nkhuyu zoipa zija zimene munthu sangadye chifukwa cha kuipa kwake,+ Yehova wanena kuti: “Momwemonso ndidzapereka Zedekiya+ mfumu ya Yuda, akalonga ake ndi anthu onse opulumuka mu Yerusalemu amene atsalira m’dzikoli,+ komanso anthu okhala m’dziko la Iguputo.+