5 Usaziweramire kapena kuzitumikira,+ chifukwa ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wofuna kuti anthu azidzipereka kwa ine ndekha,*+ wolanga ana, zidzukulu ndi ana a zidzukuluzo, chifukwa cha zolakwa za abambo a anthu odana ndi ine.+
7 Wosungira mibadwo masauzande kukoma mtima kosatha,+ wokhululukira zolakwa ndi machimo,+ koma wosalekerera konse wolakwa osam’langa.+ Wolanga ana, zidzukulu, ndi ana a zidzukuluzo chifukwa cha zolakwa za abambo awo.”+
6 Koma kunena za iwe Pasuri, ndi onse okhala m’nyumba yako, mudzapita ku ukapolo.+ Iwe udzapita ku Babulo ndipo udzafera kumeneko ndi kuikidwa m’manda komweko pamodzi ndi anzako onse,+ chifukwa walosera kwa iwo monama.’”+