14 “N’chifukwa chiyani tikungokhala? Sonkhanani pamodzi, ndipo tiyeni tilowe m’mizinda yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri+ kuti tikafere kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watiweruza kuti tife,+ ndipo akutipatsa madzi apoizoni kuti timwe+ chifukwa tachimwira Yehova.