2 “Yehova wanena kuti, ‘Ukaimirire m’bwalo la nyumba ya Yehova,+ ndipo anthu onse amene akubwera kudzalambira panyumba ya Yehova ukawauze zimene zidzachitikira mizinda yonse ya Yuda. Ukawauze mawu onse amene ndidzakulamula kuti uwauze.+ Usachotsepo mawu ngakhale amodzi.+