49 Ponena za ana a Amoni+ Yehova wanena kuti: “Kodi Isiraeli alibe ana aamuna, kapena kodi alibe wolandira cholowa? N’chifukwa chiyani Malikamu+ watenga Gadi+ kukhala cholowa chake? N’chifukwa chiyani anthu olambira Malikamu akukhala m’mizinda ya Isiraeli?”+