18 “Malire a mbali ya kum’mawa ayambire pakati pa Haurani+ ndi Damasiko+ n’kutsetsereka ndi mtsinje wa Yorodano+ pakati pa Giliyadi+ ndi dziko la Isiraeli. Anthu inu muyeze mtunda kuchokera kumalirewo kukafika kunyanja ya kum’mawa. Amenewa akhale malire a mbali ya kum’mawa.