19 Pakumveka mawu olirira thandizo a mwana wamkazi wa anthu anga ali kudziko lakutali.+ Iye akuti: “Kodi Yehova sali mu Ziyoni?+ Kapena kodi mfumu ya Yerusalemu mulibe mmenemo?”+
“N’chifukwa chiyani andikhumudwitsa ndi mafano awo ogoba, ndiponso milungu yawo yachilendo yopanda pake?”+