17 Koma Isiraeli adzapulumutsidwa chifukwa chokhala pa mgwirizano ndi Yehova+ ndipo adzakhala wopulumutsidwa mpaka kalekale.+ Anthu inu simudzachita manyazi+ ndipo simudzanyozeka+ mpaka kalekale, ngakhale kwamuyaya.
4 Usachite mantha,+ pakuti sudzachititsidwa manyazi.+ Usachite manyazi, pakuti sudzakhumudwitsidwa.+ Iwe udzaiwala ngakhale manyazi a paubwana wako,+ ndipo sudzakumbukiranso kunyozeka kwa paumasiye wako wa nthawi yaitali.”