15 Koma mudziwe kuti, mukandipha mupalamula mlandu wamagazi chifukwa chopha munthu wosalakwa. Mlanduwo ukhala pa inuyo, pamzindawu ndi pa anthu onse okhala mumzindawu+ chifukwa kunena zoona, Yehova ndi amene wandituma kuti ndidzakuuzeni mawu onsewa.”+