6 Iye ananenanso kuti: “Ndine Mulungu wa atate ako, Mulungu wa Abulahamu, Mulungu wa Isaki ndi Mulungu wa Yakobo.”+ Pamenepo Mose anaphimba nkhope yake, chifukwa anaopa kuyang’ana Mulungu woona.
13 Mulungu wa Abulahamu, wa Isaki ndi wa Yakobo,+ Mulungu wa makolo athu, ndi amene walemekeza+ Mtumiki+ wake Yesu, amene inu munamupereka+ ndi kumukana pamaso pa Pilato, Pilatoyo akufuna kumumasula.+
16 Koma tsopano akufunitsitsa malo abwino koposa, amene ndi malo akumwamba.+ Pa chifukwa chimenechi, Mulungu sachita nawo manyazi kuti azimuitana monga Mulungu wawo,+ pakuti iye wawakonzera mzinda.+