36 Komanso, anawapatsa fanizo kuti: “Palibe amene amadula chigamba pamalaya akunja atsopano n’kuchisokerera pamalaya akunja akale. Munthu akachita zimenezo, chigamba chatsopanocho chimachoka pansalu yakaleyo. Ndiponso chigamba cha nsalu yatsopanocho sichiyenerana ndi malaya akalewo.+