Mateyu
9 Chotero Yesu anakwera ngalawa n’kuwolokera tsidya lina, ndipo anapita kumzinda umene anali kukhala.+ 2 Kumeneko anthu anam’bweretsera munthu wakufa ziwalo, atagona pakabedi.+ Poona chikhulupiriro chawo, Yesu anauza wakufa ziwaloyo kuti: “Limba mtima, mwanawe, machimo ako akhululukidwa.”+ 3 Atatero, alembi ena anang’ung’udza chamumtima kuti: “Munthu ameneyu akunyoza Mulungu.”+ 4 Koma Yesu, podziwa zimene iwo anali kuganiza,+ ananena kuti: “N’chifukwa chiyani mukuganiza zinthu zoipa m’mitima mwanu?+ 5 Mwachitsanzo, chapafupi n’chiti, kunena kuti, Machimo ako akhululukidwa, kapena kunena kuti, Nyamuka uyende?+ 6 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali ndi mphamvu padziko lapansi zokhululukira machimo+ . . .” pamenepo anauza wakufa ziwalo uja kuti: “Nyamuka, tenga kabedi kakoka uzipita kwanu.”+ 7 Ndipo ananyamuka n’kupita kwawo. 8 Khamu la anthulo litaona zimenezi, linagwidwa ndi mantha ndipo linatamanda Mulungu,+ amene anapereka mphamvu zimenezo+ kwa anthu.
9 Atachoka pamenepo, Yesu anaona munthu wina wotchedwa Mateyu atakhala pansi mu ofesi yokhomera msonkho, ndipo anamuuza kuti: “Ukhale wotsatira wanga.”+ Nthawi yomweyo ananyamuka ndi kum’tsatira.+ 10 Nthawi inayake, pamene anali kudya patebulo m’nyumba ina,+ kunabwera okhometsa msonkho ndi ochimwa ambiri ndipo anayamba kudya pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake. 11 Koma poona zimenezi, Afarisi anayamba kufunsa ophunzira ake kuti: “N’chifukwa chiyani mphunzitsi wanu amadya limodzi ndi okhometsa msonkho ndi anthu ochimwa?”+ 12 Iye atamva zimenezo, anayankha kuti: “Anthu abwinobwino safuna dokotala,+ koma odwala ndi amene amamufuna. 13 Choncho pitani mukaphunzire tanthauzo la mawu akuti, ‘Ndikufuna chifundo, osati nsembe.’+ Chifukwa ine sindinabwere kudzaitana anthu olungama, koma ochimwa.”
14 Kenako ophunzira a Yohane anabwera kwa iye n’kumufunsa kuti: “N’chifukwa chiyani ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”+ 15 Yesu anawayankha kuti: “Anzake a mkwati samva chisoni ngati mkwatiyo+ ali nawo limodzi, si choncho kodi? Koma masiku adzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa+ pakati pawo, ndipo pa nthawiyo adzasala kudya.+ 16 Palibe amene amasokerera chigamba cha nsalu yatsopano pamalaya akunja akale. Pakuti mphamvu yonse ya chigambacho ingakoke ndi kung’amba malayawo ndipo kung’ambikako kungawonjezeke kwambiri.+ 17 Ndiponso anthu sathira vinyo watsopano m’matumba achikopa akale. Akachita zimenezo, matumba achikopawo amaphulika ndipo vinyoyo amatayika moti matumbawo amawonongeka.+ Koma anthu amathira vinyo watsopano m’matumba achikopa atsopano, ndipo zonse ziwirizo zimasungika bwino.”+
18 Pamene anali kuwauza zimenezi, wolamulira wina+ anam’yandikira. Kenako anamugwadira+ n’kunena kuti: “Panopa mwana wanga wamkazi ayenera kuti wamwalira kale.+ Koma tiyeni mukamukhudze ndi dzanja lanu ndipo akhala ndi moyo.”+
19 Pamenepo Yesu ananyamuka ndi kumutsatira. Ophunzira ake anachitanso chimodzimodzi. 20 Tsopano mayi wina amene anali ndi nthenda yotaya magazi kwa zaka 12+ anafika kumbuyo kwake n’kugwira ulusi wopota wa m’mphepete mwa malaya ake akunja,+ 21 chifukwa mumtima mwake anali kunena kuti: “Ndikangogwira malaya ake akunja okhawo, ndichira ndithu.”+ 22 Yesu anatembenuka, ndipo anaona mayiyo n’kunena kuti: “Mwanawe, limba mtima, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.”+ Kuchokera pa ola limenelo mayiyo anachira.+
23 Tsopano atalowa m’nyumba ya wolamulira uja,+ anaona oliza zitoliro komanso khamu la anthu likubuma.+ 24 Yesu anawauza kuti: “Tulukani muno, pakuti mtsikanayu sanamwalire ayi, koma akugona.”+ Atanena zimenezi, anthuwo anayamba kum’seka monyodola.+ 25 Atatulutsa anthu aja panja, iye analowa ndi kugwira dzanja la mtsikanayo,+ ndipo iye anadzuka.+ 26 Nkhani imeneyi inamveka m’dera lonselo.
27 Pamene Yesu anali kudutsa kuchokera kumeneko, anthu awiri akhungu+ anam’tsatira. Iwo anafuula ndi kunena kuti: “Mutichitire chifundo,+ Mwana wa Davide.” 28 Yesu atalowa m’nyumba, anthu akhunguwo anabwera kwa iye, ndipo anawafunsa kuti: “Kodi muli ndi chikhulupiriro+ kuti ndingachite zimenezi?” Iwo anamuyankha kuti: “Inde, Ambuye.” 29 Kenako anawagwira m’maso,+ n’kunena kuti: “Malinga ndi chikhulupiriro chanu zichitike momwemo kwa inu,” 30 ndipo maso awo anatseguka. Chotero Yesu anawalamula mwamphamvu kuti: “Samalani, aliyense asadziwe zimenezi.”+ 31 Koma iwo, atatuluka kunja, anafalitsa za iye ponseponse m’dera limenelo.+
32 Tsopano pamene iwo anali kunyamuka, anthu anam’bweretsera munthu wosalankhula wogwidwa ndi chiwanda.+ 33 Atatulutsa chiwandacho, munthu wosalankhulayo analankhula,+ moti khamu la anthulo linadabwa+ ndipo linanena kuti: “Zinthu zoterezi sizinaonekepo n’kale lonse mu Isiraeli.” 34 Koma Afarisi anayamba kunena kuti: “Ameneyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya wolamulira ziwanda.”+
35 Tsopano Yesu anayamba ulendo woyendera mizinda ndi midzi yonse. Anali kuphunzitsa m’masunagoge awo, kulalikira uthenga wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa matenda amtundu uliwonse ndi zofooka zilizonse.+ 36 Poona chikhamu cha anthu, iye anawamvera chisoni,+ chifukwa anali onyukanyuka ndi otayika ngati nkhosa zopanda m’busa.+ 37 Pamenepo anauza ophunzira ake kuti: “Inde, zokolola n’zochuluka, koma antchito ndi ochepa.+ 38 Choncho pemphani Mwini zokolola kuti atumize antchito kukakolola.”+