27 “‘Ufumu, ulamuliro, ndi ulemerero wa maufumu a padziko lonse lapansi zinaperekedwa kwa oyera a Wamkulukulu.+ Ufumu wawo+ udzakhalapo mpaka kalekale ndipo maulamuliro onse adzawatumikira ndi kuwamvera.’+
8 “Koma iwe nsanja ya gulu la nkhosa, malo okwera a mwana wamkazi wa Ziyoni,+ ulamuliro udzabwerera kwa iwe. Ulamuliro woyamba, ufumu wa mwana wamkazi wa Yerusalemu,+ udzabwerera kwa iwe.+