11 Ndipo Mulungu anapatsa Abulahamu mdulidwe monga chizindikiro.+ Chizindikiro chimenechi chinali chosonyeza kuti, chifukwa cha chikhulupiriro, Mulungu anamuyesa wolungama asanadulidwe, kuti adzakhale tate+ wa onse osadulidwa okhala ndi chikhulupiriro,+ kuti anthuwo adzaonedwe kuti ndi olungama.