14 Inde, kuti tisakhalenso tiana, otengekatengeka+ ngati kuti tikukankhidwa ndi mafunde, ndiponso otengeka kupita uku ndi uku ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso+ chonyenga+ cha anthu, mwa kuchenjera kwa anthu popeka mabodza.
8 Samalani: mwina wina angakugwireni+ ngati nyama, mwa nzeru za anthu+ ndi chinyengo chopanda pake,+ malinga ndi miyambo ya anthu, malinganso ndi mfundo zimene zili maziko a moyo wa m’dzikoli,+ osati malinga ndi Khristu,