14 Weta anthu ako ndi ndodo yako.+ Weta gulu la nkhosa zomwe ndi cholowa chako, zimene zinali kukhala zokhazokha m’nkhalango pakati pa mitengo ya zipatso.+ Uzilole kuti zikadyere ku Basana ndi ku Giliyadi+ ngati mmene zinali kuchitira masiku akale.+
28 Mukhale tcheru ndi kuyang’anira+ gulu lonse la nkhosa,+ limene mzimu woyera wakuikani pakati pawo kukhala oyang’anira,+ kuti muwete mpingo wa Mulungu,+ umene anaugula ndi magazi+ a Mwana wake weniweni.