13 Ndipo cholengedwa chilichonse chakumwamba, padziko lapansi,+ pansi pa nthaka, panyanja, ndi zinthu zonse za mmenemo, ndinazimva zikunena kuti: “Iye wokhala pampando wachifumu,+ ndi Mwanawankhosa,+ atamandidwe ndiponso alandire ulemu,+ ulemerero,+ ndi mphamvu, kwamuyaya.”