4 Pakati pa anthu amenewa, mulungu wa nthawi* ino+ wachititsa khungu maganizo a anthu osakhulupirira,+ kuti asaone+ kuwala+ kwa uthenga wabwino waulemerero+ wonena za Khristu, yemwe ali chifaniziro+ cha Mulungu.
2 Munali kuyenda m’zimenezo mogwirizana ndi nthawi*+ za m’dzikoli, momveranso wolamulira+ wa mpweya umene umalamulira zochita za anthu. Mpweya umenewu, kapena kuti kaganizidwe kameneka,+ tsopano kakugwira ntchito mwa ana a kusamvera.+