Malaki 2:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Chifukwa ine ndimadana ndi zoti anthu azithetsa mabanja,”+ watero Yehova Mulungu wa Isiraeli. “Ndimadana ndi munthu wankhanza.* Samalani kuti mukhale ndi maganizo oyenera ndipo musamachite zachinyengo,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba. Mateyu 19:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 nʼkunena kuti: ‘Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake nʼkudziphatika kwa mkazi wake ndipo awiriwo adzakhala thupi limodziʼ?+ Maliko 10:7, 8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake,+ 8 ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi,’+ moti sakhalanso kuti ndi awiri koma thupi limodzi. Aroma 7:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Mwachitsanzo, mkazi wokwatiwa amakhala womangidwa kwa mwamuna wake mwalamulo pamene mwamunayo ali moyo. Koma mwamunayo akamwalira, mkazi amakhala womasuka ku lamulo lokhudza mwamuna wake.+ 1 Akorinto 6:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Kodi inu simukudziwa kuti amene wagonana ndi hule amakhala thupi limodzi ndi huleyo? Chifukwa anati, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.”+ Aefeso 5:31 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 “Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake nʼkudziphatika kwa* mkazi wake ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”+ Aheberi 13:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Ukwati ukhale wolemekezeka kwa onse, ndipo pogona pa anthu okwatirana pakhale posadetsedwa,+ chifukwa Mulungu adzaweruza achiwerewere* ndiponso achigololo.+
16 Chifukwa ine ndimadana ndi zoti anthu azithetsa mabanja,”+ watero Yehova Mulungu wa Isiraeli. “Ndimadana ndi munthu wankhanza.* Samalani kuti mukhale ndi maganizo oyenera ndipo musamachite zachinyengo,”+ watero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.
5 nʼkunena kuti: ‘Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake nʼkudziphatika kwa mkazi wake ndipo awiriwo adzakhala thupi limodziʼ?+
7 Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake,+ 8 ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi,’+ moti sakhalanso kuti ndi awiri koma thupi limodzi.
2 Mwachitsanzo, mkazi wokwatiwa amakhala womangidwa kwa mwamuna wake mwalamulo pamene mwamunayo ali moyo. Koma mwamunayo akamwalira, mkazi amakhala womasuka ku lamulo lokhudza mwamuna wake.+
16 Kodi inu simukudziwa kuti amene wagonana ndi hule amakhala thupi limodzi ndi huleyo? Chifukwa anati, “Awiriwo adzakhala thupi limodzi.”+
31 “Chifukwa cha zimenezi mwamuna adzasiya bambo ake ndi mayi ake nʼkudziphatika kwa* mkazi wake ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”+
4 Ukwati ukhale wolemekezeka kwa onse, ndipo pogona pa anthu okwatirana pakhale posadetsedwa,+ chifukwa Mulungu adzaweruza achiwerewere* ndiponso achigololo.+