Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 30:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Komanso Aroni akamayatsa nyalezo madzulo, aziwotcha zofukizazo. Zimenezi ndi zofukiza zoyenera kuperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mʼmibadwo yanu yonse.

  • Levitiko 24:2, 3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Lamula Aisiraeli kuti akubweretsere mafuta ounikira oyenga bwino kwambiri a maolivi, kuti nyale ziziyaka nthawi zonse.+ 3 Aroni azikhazika nyale kunja kwa katani ya Malo Oyera Koposa mʼchihema chokumanako. Nyalezo ziziunikira pamaso pa Yehova nthawi zonse kuyambira madzulo mpaka mʼmawa. Limeneli ndi lamulo kwa inu mpaka kalekale mʼmibadwo yanu yonse.

  • Numeri 8:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Lankhula ndi Aroni ndipo umuuze kuti, ‘Ukayatsa nyale, nyale zonse 7 ziziunikira malo apatsogolo pa choikapo nyalecho.’”+

  • 2 Mbiri 13:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Iwo akupereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼmawa uliwonse+ ndi madzulo alionse limodzi ndi mafuta onunkhira.+ Ndipo mikate yosanjikiza*+ ili patebulo la golide woyenga bwino. Komanso madzulo alionse+ amayatsa nyale zomwe zili pachoikapo nyale chagolide.+ Tikuchita zimenezi chifukwa tikukwaniritsa udindo wathu kwa Yehova Mulungu wathu, koma inuyo mwamusiya.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena