-
Levitiko 1:4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Iye aziika dzanja lake pamutu pa nsembe yopserezayo ndipo idzalandiridwa kuti iphimbe machimo ake.
-
-
Levitiko 8:18-21Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
18 Kenako anatenga nkhosa yamphongo ya nsembe yopsereza ndipo Aroni ndi ana ake anaika manja awo pamutu pa nkhosayo.+ 19 Ndiyeno Mose anapha nkhosayo nʼkuwaza magazi ake mbali zonse za guwa lansembe. 20 Anaduladula nkhosayo ndipo Mose anatenga mutu wake, nyama yoduladulayo ndi mafuta ake,* nʼkuziwotcha. 21 Anatsuka matumbo ndi ziboda ndipo Mose anawotcha paguwa lansembe nkhosa yonseyo. Inali nsembe yopsereza yakafungo kosangalatsa.* Komanso inali nsembe yowotcha pamoto yoperekedwa kwa Yehova, mogwirizana ndi zimene Yehova analamula Mose.
-