Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 29:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Zimene uzipereka paguwa lansembelo ndi izi: ana a nkhosa a chaka chimodzi, awiri pa tsiku ndipo uzichita zimenezi nthawi zonse.+

  • Ekisodo 29:42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 42 Mʼmibadwo yanu yonse, muzipereka nsembe yopsereza imeneyi nthawi zonse pakhomo la chihema chokumanako pamaso pa Yehova, kumene ndidzaonekera kwa inu kuti ndilankhule nanu.+

  • 2 Mbiri 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ine ndikumanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wanga kuti ikhale yopatulika kwa iye. Ndikufuna kuti ndiziperekamo nsembe za mafuta onunkhira pamaso pake+ ndiponso kuti nthawi zonse muzikhala mkate wosanjikiza.*+ Ndiziperekamonso nsembe zopsereza mʼmawa ndi madzulo,+ pa Masabata,+ masiku amene mwezi watsopano waoneka+ ndi pa nthawi ya zikondwerero+ za Yehova Mulungu wathu. Aisiraeli afunika azichita zimenezi mpaka kalekale.

  • Ezara 3:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Iwo anamanga guwa lansembe pamalo ake akale ngakhale kuti ankaopa anthu a mitundu ina yowazungulira.+ Atatero anayamba kuperekerapo nsembe zopsereza kwa Yehova, zamʼmawa ndi zamadzulo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena