Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 16:39, 40
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 39 Choncho wansembe Eleazara anatenga zofukizira zakopa zimene anthu amene anapsa ndi moto aja anabweretsa, ndipo anazisula nʼkupanga timalata tokutira guwa lansembe, 40 mogwirizana ndi zimene Yehova anamuuza kudzera mwa Mose. Timalatato tinali chikumbutso kwa Aisiraeli kuti munthu wamba* amene si mbadwa ya Aroni asayandikire kwa Yehova kuti akapereke nsembe zofukiza.+ Anachita zimenezi kuti pasapezeke wina aliyense wochita zimene Kora limodzi ndi anthu amene ankamutsatira anachita.+

  • 1 Samueli 6:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Koma Mulungu anapha anthu a ku Beti-semesi chifukwa anayangʼana Likasa la Yehova. Anapha anthu 50,070* ndipo anthu anayamba kulira chifukwa Yehova anapha anthu ambiri.+

  • 2 Mbiri 26:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Koma atangokhala wamphamvu, mtima wake unayamba kudzikuza mpaka kufika pomʼpweteketsa. Iye anachita zosakhulupirika kwa Yehova Mulungu wake ndipo anapita mʼkachisi wa Yehova kukapereka nsembe zofukiza paguwa lansembe.+

  • 2 Mbiri 26:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Iwo anapita pamene panali Mfumu Uziya kukamuletsa. Anamuuza kuti: “Mfumu Uziya, si zoyenera kuti inuyo mupereke nsembe zofukiza kwa Yehova.+ Ansembe okha ndi amene ayenera kupereka nsembe zofukiza chifukwa ndi mbadwa za Aroni+ ndipo anayeretsedwa. Tulukani mʼnyumba yopatulikayi popeza mwachita zosakhulupirika ndipo zimenezi sizikubweretserani ulemerero wochokera kwa Yehova Mulungu.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena