15 Kenako azipha mbuzi ya nsembe yamachimo yoperekera anthuwo,+ nʼkulowa ndi magazi ake kuchipinda, kuseri kwa katani.+ Kumeneko magaziwo+ azichita nawo zimene anachita ndi magazi a ngʼombe yamphongo ija. Azidontheza magaziwo patsogolo pa chivundikiro.