Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 4:13-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Kenako atachoka ku Nazareti, anafika ku Kaperenao+ nʼkupeza malo okhala mʼmbali mwa nyanja mʼzigawo za Zebuloni ndi Nafitali, 14 kuti mawu amene Mulungu ananena kudzera mwa mneneri Yesaya akwaniritsidwe. Iye ananena kuti: 15 “Anthu amene akukhala mʼdziko la Zebuloni ndi dziko la Nafitali, mʼmbali mwa msewu wakunyanja kutsidya lina la Yorodano, ku Galileya kumene kunkakhala anthu a mitundu ina, 16 anthu amene ankakhala mumdima anaona kuwala kwakukulu, ndipo anthu amene ankakhala mʼdera lamthunzi wa imfa, kuwala+ kunawaunikira.”+

  • Luka 1:78, 79
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 78 chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu. Ndi chifundo chimenechi, kuwala kwamʼmawa kudzatifikira kuchokera kumwamba, 79 ndipo kudzaunikira amene akukhala mumdima komanso mumthunzi wa imfa+ ndi kutsogolera mapazi athu panjira yamtendere.”

  • Luka 2:30-32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 chifukwa maso anga aona njira yanu yopulumutsira anthu+ 31 imene mwakonza pamaso pa anthu a mitundu yonse.+ 32 Maso anga aona kuwala+ kochotsa nsalu yophimba imene ikulepheretsa mitundu ya anthu kuti isamaone,+ komanso ndaona ulemerero wa anthu anu Aisiraeli.”

  • Yohane 1:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Kuwala kwenikweni kumene kumaunikira anthu osiyanasiyana kunali kutatsala pangʼono kubwera mʼdziko.+

  • Yohane 8:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 12 Kenako Yesu analankhula nawonso kuti: “Ine ndine kuwala kwa dziko.+ Aliyense wonditsatira ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala ndi kuwala+ kwa moyo.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena