Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 12:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ine ndidzadutsa mʼdziko la Iguputo usiku umenewo nʼkupha mwana aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Iguputo, mwana wa munthu kapena wa chiweto.+ Ndipo ndidzapereka chiweruzo pa milungu yonse ya mu Iguputo.+ Ine ndine Yehova.

  • Yesaya 19:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Uwu ndi uthenga wokhudza Iguputo:+

      Taonani! Yehova wakwera mtambo wothamanga ndipo akubwera mu Iguputo.

      Milungu yopanda pake ya ku Iguputo idzanjenjemera pamaso pake,+

      Ndipo mitima ya anthu a ku Iguputo idzachita mantha kwambiri.

  • Yeremiya 43:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Nyumba za milungu* ya ku Iguputo ndidzaziwotcha ndi moto.+ Nebukadinezara adzawotcha nyumbazo nʼkutenga milunguyo kupita nayo kudziko lina. Mʼbusa savutika kuvala chovala chake. Mofanana ndi zimenezi, Nebukadinezara sadzavutika kugonjetsa dziko la Iguputo nʼkuchokako mwamtendere.* 13 Iye adzaphwanyaphwanya zipilala za ku Beti-semesi,* mzinda umene uli ku Iguputo. Ndipo nyumba za milungu* ya ku Iguputo adzaziwotcha ndi moto.”’”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena