-
Yeremiya 28:1-4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
28 Ndiyeno mʼchaka chomwecho, chaka cha 4, mʼmwezi wa 5, kumayambiriro kwa ulamuliro wa Zedekiya+ mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, wa ku Gibiyoni,+ anauza Yeremiya mʼnyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti: 2 “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Ndithyola goli la mfumu ya Babulo.+ 3 Zaka ziwiri zisanathe, ndibwezeretsa pamalo ano ziwiya zonse zamʼnyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya Babulo anatenga kuno nʼkupita nazo ku Babulo.’”+ 4 “‘Ndipo Yekoniya+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, ndiponso anthu onse a mu Yuda amene anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo+ ndiwabwezeretsa kuno, chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya Babulo,’ akutero Yehova.”
-