Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 6:13, 14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Chifukwa aliyense kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, akupeza phindu mwachinyengo.+

      Kuyambira mneneri mpaka wansembe, aliyense akuchita zachinyengo.+

      14 Iwo akuyesa kuchiritsa mwachinyengo kuwonongeka kwa anthu anga* ponena kuti,

      ‘Kuli mtendere! Kuli mtendere!’

      Pamene kulibe mtendere.+

  • Yeremiya 28:1-4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Ndiyeno mʼchaka chomwecho, chaka cha 4, mʼmwezi wa 5, kumayambiriro kwa ulamuliro wa Zedekiya+ mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, wa ku Gibiyoni,+ anauza Yeremiya mʼnyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti: 2 “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Ndithyola goli la mfumu ya Babulo.+ 3 Zaka ziwiri zisanathe, ndibwezeretsa pamalo ano ziwiya zonse zamʼnyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya Babulo anatenga kuno nʼkupita nazo ku Babulo.’”+ 4 “‘Ndipo Yekoniya+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, ndiponso anthu onse a mu Yuda amene anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babulo+ ndiwabwezeretsa kuno, chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya Babulo,’ akutero Yehova.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena