Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 25:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Ndiyeno Esau anapempha Yakobo kuti: “Chonde, fulumira ndigawireko pangʼono mphodza zofiira zimene ukuphikazo,* ndatopatu ine!”* Nʼchifukwa chake anamupatsa dzina lakuti Edomu.*+

  • Yesaya 34:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  5 “Chifukwa lupanga langa lidzakhala magazi okhaokha kumwambako.+

      Lupangalo lidzatsikira pa Edomu kuti lipereke chiweruzo,+

      Lidzatsikira pa anthu amene ndikufuna kuwawononga.

  • Ezekieli 25:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: ‘Edomu wabwezera zoipa kwa nyumba ya Yuda ndipo wapalamula mlandu waukulu chifukwa chowabwezera.+ 13 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Nditambasulanso dzanja langa nʼkulanga Edomu ndipo ndipha anthu ndi ziweto mʼdzikolo, moti ndidzalisandutsa bwinja.+ Anthu adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Temani mpaka ku Dedani.+

  • Amosi 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Yehova wanena kuti,

      ‘Chifukwa Edomu wandigalukira mobwerezabwereza,+ sindidzamusinthira chigamulo changa.

      Chifukwa anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga,+

      Komanso anakana kusonyeza chifundo.

      Anapitiriza kuwakhadzulakhadzula,

      Ndipo anapitirizabe kuwakwiyira kwambiri.+

  • Obadiya 1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 1 Awa ndi masomphenya a Obadiya:*

      Zimene Yehova Ambuye Wamkulu Koposa akunena zokhudza Edomu+ ndi izi:

      “Ife tamva uthenga wochokera kwa Yehova,

      Ndipo nthumwi yatumidwa kwa anthu amitundu ina kukanena kuti:

      ‘Konzekani! Tiyeni tikamenyane naye.’”+

  • Malaki 1:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Ngakhale kuti Edomu akunena kuti, ‘Ife tawonongedwa, koma tibwerera nʼkukamanga malo athu owonongedwawo,’ Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti, ‘Iwo apita kukamanga, koma ine ndikagwetsa. Anthu adzatchula malo awowo kuti “dera la zoipa” ndipo iwowo adzatchedwa “anthu okanidwa ndi Yehova mpaka kalekale.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena