Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 19:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Yesu anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, pa nthawi ya kulenganso zinthu, Mwana wa munthu adzakhala pampando wake wachifumu waulemerero, inu amene mwakhala mukunditsatira mudzakhalanso mʼmipando yachifumu 12, nʼkumaweruza mafuko 12 a Isiraeli.+

  • Luka 22:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Choncho ndikuchita nanu pangano, mofanana ndi mmene Atate wanga wachitira pangano la ufumu ndi ine,+

  • Chivumbulutso 1:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 nʼkutipanga kukhala mafumu+ ndi ansembe+ kuti titumikire Mulungu wake ndi Atate wake, kwa iyeyo kukhale ulemerero ndi mphamvu kwamuyaya. Ame.

  • Chivumbulutso 3:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Amene wapambana pankhondo+ ndidzamulola kuti akhale ndi ine pampando wanga wachifumu,+ ngati mmene ine ndinakhalira+ ndi Atate wanga pampando wawo wachifumu nditapambana pankhondo.

  • Chivumbulutso 5:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iwo ankaimba nyimbo yatsopano+ yakuti: “Inu ndinu woyenera kutenga mpukutuwo ndi kumatula zidindo zake zomatira, chifukwa munaphedwa ndipo ndi magazi anu munagula anthu kuti atumikire Mulungu.+ Anthuwo ndi ochokera mu fuko lililonse, chilankhulo chilichonse, mtundu uliwonse ndi dziko lililonse.+ 10 Ndipo munawapanga kuti akhale mafumu+ ndi ansembe a Mulungu wathu,+ moti adzakhala mafumu+ olamulira dziko lapansi.”

  • Chivumbulutso 20:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Kenako ndinaona mipando yachifumu ndipo amene anakhala pamipandoyo anapatsidwa mphamvu zoweruza. Ndinaona miyoyo ya anthu amene anaphedwa chifukwa chochitira umboni za Yesu komanso chifukwa cholankhula za Mulungu. Inde, ndinaona miyoyo ya anthu amene sanalambire chilombo kapena chifaniziro chake ndipo sanalandire chizindikiro pazipumi zawo ndi padzanja lawo.+ Iwo anakhalanso ndi moyo ndipo analamulira monga mafumu limodzi ndi Khristu+ kwa zaka 1,000.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena