Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 34:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Ndiyeno Yehova anadutsa pamaso pa Mose akulengeza kuti: “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo+ ndi wokoma mtima,*+ wosakwiya msanga+ ndiponso wachikondi chokhulupirika chochuluka+ komanso choonadi.*+

  • Numeri 14:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 ‘Yehova ndi wosakwiya msanga, ndiponso wachikondi chokhulupirika chochuluka.*+ Amakhululukira zolakwa ndi machimo, koma sadzalekerera wolakwa osamupatsa chilango. Amalanga ana, zidzukulu ndi ana a zidzukuluzo chifukwa cha zolakwa za abambo awo.’+

  • Nehemiya 9:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Iwo anakana kumvera+ ndipo sanakumbukire zinthu zodabwitsa zimene munawachitira. Mʼmalomwake anaumitsa khosi ndipo anasankha munthu woti awatsogolere pobwereranso ku ukapolo ku Iguputo.+ Koma inu ndinu Mulungu wokonzeka kukhululuka, wachisomo, wachifundo, wosakwiya msanga ndiponso wachikondi chokhulupirika*+ chochuluka, choncho simunawasiye.+

  • Salimo 106:44, 45
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Koma Mulungu ankaona mavuto amene akukumana nawo+

      Ndipo ankamva kulira kwawo kopempha thandizo.+

      45 Pofuna kuwathandiza iye ankakumbukira pangano lake,

      Ndipo ankawamvera chisoni* chifukwa cha chikondi chake chokhulupirika chomwe ndi chachikulu.*+

  • Mika 7:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Kodi pali Mulungu winanso wofanana ndi inu,

      Amene amakhululukira zolakwa ndi machimo+ a anthu ake otsala omwe ndi cholowa chake?+

      Inu simudzakhalabe wokwiya mpaka kalekale,

      Chifukwa mumakonda chikondi chokhulupirika.+

      19 Inu mudzatichitiranso chifundo+ ndipo mudzagonjetsa* zolakwa zathu.

      Machimo athu onse mudzawaponya mʼnyanja pamalo ozama.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena