Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Machitidwe 8:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Saulo anayamba kuzunza mpingo mwankhanza. Ankalowa mʼnyumba iliyonse nʼkumakokera panja amuna ndi akazi omwe, ndipo ankawapititsa kundende.+

  • Machitidwe 22:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Ndinkazunza otsatira Njira imeneyi mpaka kuwapha. Ndinkamanga amuna ndi akazi nʼkukawapereka kundende.+

  • Machitidwe 26:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndipo izi ndi zimene ndinachitadi ku Yerusalemu. Ndinkatsekera mʼndende oyera ambiri+ nditapatsidwa mphamvu ndi ansembe aakulu.+ Akaweruzidwa kuti aphedwe, ine ndinkavomereza. 11 Nthawi zambiri ndinkawapatsa chilango mʼmasunagoge onse, pofuna kuwakakamiza kuti asiye zimene amakhulupirira. Popeza ndinali nditakwiya nawo kwambiri, ndinafika powazunza ngakhale mʼmizinda yakunja.

  • Agalatiya 1:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Munamva ndithu zimene ndinkachita ndili mʼChiyuda,+ kuti ndinkazunza kwambiri mpingo wa Mulungu ndipo ndinapitiriza kuuwononga.+

  • 1 Timoteyo 1:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye wathu, amene anandipatsa mphamvu nʼkundipatsanso utumiki chifukwa anaona kuti ndine wokhulupirika.+ 13 Anatero ngakhale kuti kale ndinali wonyoza Mulungu, wozunza anthu ake ndiponso wachipongwe.+ Komabe anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita zinthu mosadziwa komanso ndinalibe chikhulupiriro.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena