Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Luka 4:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Poyankha Yesu anamuuza kuti: “Malemba amati, ‘Yehova* Mulungu wako ndi amene uyenera kumulambira ndipo uyenera kutumikira iye yekha basi.’”+

  • Machitidwe 14:12-15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Choncho Baranaba anayamba kumutchula kuti Zeu, koma Paulo ankamutchula kuti Heme, chifukwa ndi amene ankatsogolera polankhula. 13 Ndiyeno wansembe wa Zeu, amene kachisi wake anali pafupi ndi polowera mumzindawo, anabweretsa ngʼombe zamphongo ndi nkhata zamaluwa pamageti. Iye ankafuna kupereka nsembe pamodzi ndi gulu la anthulo.

      14 Koma atumwiwo, Baranaba ndi Paulo, atamva zimenezi anangʼamba malaya awo akunja nʼkuthamanga kukalowa mʼgulu la anthu lija akufuula kuti: 15 “Anthu inu, mukuchitiranji zimenezi? Ifenso ndife anthu okhala ndi zofooka ngati inu nomwe.+ Tikulengeza uthenga wabwino kwa inu kuti musiye zinthu zachabechabezi nʼkuyamba kulambira Mulungu wamoyo, amene anapanga kumwamba, dziko lapansi, nyanja ndi zonse zokhala mmenemo.+

  • Chivumbulutso 19:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Zitatero ndinagwada pansi nʼkuwerama patsogolo pa mapazi ake kuti ndimulambire. Koma iye anandiuza kuti: “Samala! Usachite zimenezo!+ Inetu ndangokhala kapolo mnzako ndi wa abale ako amene ali ndi ntchito yochitira umboni za Yesu.+ Lambira Mulungu,+ chifukwa cholinga cha maulosi ndi kuchitira umboni zokhudza Yesu.”+

  • Chivumbulutso 22:8, 9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Ine Yohane, ndi amene ndinamva komanso kuona zinthu zimenezi. Nditamva komanso kuona zinthu zimenezi, ndinagwada nʼkuwerama pamapazi a mngelo amene ankandionetsa zinthu zimenezi kuti ndimulambire. 9 Koma iye anandiuza kuti: “Samala! Usachite zimenezo! Inetu ndangokhala kapolo mnzako, kapolo wa aneneri amene ndi abale ako komanso wa anthu amene akutsatira mawu amumpukutu umenewu. Lambira Mulungu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena