-
Chivumbulutso 22:8, 9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Ine Yohane, ndi amene ndinamva komanso kuona zinthu zimenezi. Nditamva komanso kuona zinthu zimenezi, ndinagwada nʼkuwerama pamapazi a mngelo amene ankandionetsa zinthu zimenezi kuti ndimulambire. 9 Koma iye anandiuza kuti: “Samala! Usachite zimenezo! Inetu ndangokhala kapolo mnzako, kapolo wa aneneri amene ndi abale ako komanso wa anthu amene akutsatira mawu amumpukutu umenewu. Lambira Mulungu.”+
-