Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 9:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Koma musadye+ nyama limodzi ndi magazi ake,+ chifukwa magaziwo ndi moyo wake.

  • Levitiko 3:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Musamadye mafuta kapena magazi alionse.+ Limeneli ndi lamulo ku mibadwo yanu yonse mpaka kalekale, kulikonse kumene mungakhale.’”

  • Levitiko 7:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Musamadye magazi alionse+ kulikonse kumene mungakhale, kaya akhale magazi a mbalame kapena a nyama.

  • Levitiko 17:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Munthu aliyense wamʼnyumba ya Isiraeli kapena mlendo wokhala pakati panu, akadya magazi alionse,+ ndidzadana naye ndipo ndidzamupha kuti asakhalenso pakati pa anthu a mtundu wake.

  • Levitiko 17:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ngati munthu wa Chiisiraeli kapena mlendo amene akukhala pakati panu wapita kokasaka, ndipo wagwira nyama kapena mbalame imene munaloledwa kuti muzidya, azithira magazi ake pansi+ nʼkuwakwirira ndi dothi.

  • Levitiko 19:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Musamadye chilichonse chimene chili ndi magazi.+

      Musamaombeze kapena kuchita zamatsenga.+

  • Deuteronomo 12:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Koma mungokhala otsimikiza mtima kuti musadye magazi,+ chifukwa magazi ndi moyo,+ ndipo musamadye nyama limodzi ndi moyo wake.

  • Deuteronomo 15:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Koma musamadye magazi ake.+ Muziwathira pansi ngati madzi.”+

  • 1 Samueli 14:32, 33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Zitatero, anthuwo anayamba kuthamangira zinthu za adani awowo mosusuka ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana a ngʼombe. Ankaziphera pansi ndipo ankadya nyamayo pamodzi ndi magazi ake.+ 33 Ndiyeno anthu ena anauza Sauli kuti: “Anthutu akuchimwira Yehova. Akudya nyama pamodzi ndi magazi ake.”+ Iye anati: “Mwachita zinthu mopanda chikhulupiriro. Gubuduzani chimwala mubwere nacho kuno mwamsanga.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena