-
Yeremiya 31:31-34Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 “Taonani! Masiku akubwera, pamene ndidzachita pangano latsopano ndi nyumba ya Isiraeli komanso nyumba ya Yuda,” akutero Yehova.+ 32 “Koma silidzakhala pangano lofanana ndi limene ndinachita ndi makolo awo, pa tsiku limene ndinagwira dzanja lawo kuti ndiwatulutse mʼdziko la Iguputo.+ ‘Pangano langa limenelo analiphwanya+ ngakhale kuti ine ndinali mbuye wawo* weniweni,’ akutero Yehova.”
33 “Pangano limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili: Ndidzaika chilamulo changa mwa iwo+ ndipo ndidzachilemba mumtima mwawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,” akutero Yehova.+
34 “Munthu sadzaphunzitsanso mnzake kapena mʼbale wake kuti, ‘Mumʼdziwe Yehova!’+ chifukwa aliyense adzandidziwa kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,”+ akutero Yehova. “Ine ndidzawakhululukira zolakwa zawo ndipo machimo awo sindidzawakumbukiranso.”+
-