Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 26:27, 28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Kenako anatenga kapu ya vinyo ndipo atayamika, anaipereka kwa iwo nʼkunena kuti: “Imwani nonsenu.+ 28 Vinyoyu akuimira ‘magazi anga+ a pangano,’+ amene adzakhetsedwe chifukwa cha anthu ambiri+ kuti machimo awo akhululukidwe.+

  • Luka 22:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Anachitanso chimodzimodzi ndi kapu atadya chakudya chamadzulocho. Iye anati: “Kapu iyi ikuimira pangano latsopano+ limene linakhazikitsidwa pogwiritsa ntchito magazi anga,+ amene adzakhetsedwe chifukwa cha inu.+

  • 1 Akorinto 11:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Anachitanso chimodzimodzi ndi kapu+ atadya chakudya chamadzulo, ndipo anati: “Kapu iyi ikuimira pangano latsopano+ limene linakhazikitsidwa pogwiritsa ntchito magazi anga.+ Muzichita zimenezi mukamamwa zamʼkapu imeneyi pondikumbukira.”+

  • Aheberi 8:8-12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Chifukwa Mulungu akuona kuti anthu akulakwitsa zinazake choncho iye akunena kuti: “‘Taonani! Masiku akubwera pamene ndidzachita pangano latsopano ndi nyumba ya Isiraeli komanso ndi nyumba ya Yuda,’ akutero Yehova.* 9 ‘Koma silidzakhala pangano lofanana ndi limene ndinachita ndi makolo awo pa tsiku limene ndinagwira dzanja lawo kuti ndiwatulutse mʼdziko la Iguputo.+ Popeza sanapitirize kusunga pangano langalo, ndinasiya kuwasamalira,’ akutero Yehova.”*

      10 “‘Pangano limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili: Ndidzaika malamulo anga mʼmaganizo mwawo ndiponso kuwalemba mʼmitima yawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,’+ akutero Yehova.*

      11 ‘Munthu sadzaphunzitsanso nzika inzake kapena mʼbale wake kuti, “Mumʼdziwe Yehova!”* Chifukwa aliyense adzandidziwa kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. 12 Ine ndidzawachitira chifundo pa zochita zawo zosalungama, ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.’”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena